Welcome to Channel AFRICA

The African
Beat, Beauty
& Strength

Today's Line Up

Here’s today’s lineup on Channel Africa, based on the official schedule:

Afro Republic
00:00 - 03:00

Afro Republic

Previous
GO TO SHOW
Morning Reset
03:00 - 06:00

Morning Reset

Previous
GO TO SHOW
Rise and Shine
06:00 - 09:00

Rise and Shine

Previous
GO TO SHOW
On The Move
09:00 - 12:00

On The Move

Previous
GO TO SHOW

Your Favorites

Your favourite in one place — stay updated and in the running.

competition Banner Alt

Enter exciting contests and giveaways. Stay tuned for chances to win exclusive Channel Africa merchandise and experiences.

Podcast Banner Alt (1)

Explore African rhythms, curated playlists, and artist spotlights from across the continent. Celebrate the sound of Africa with curated playlists.

Image Banner Shows alt

Catch your favourite programs live or on-demand. From current affairs to cultural deep-dives, there’s something for every listener.

Podcast Banner Alt

Listen to thought-provoking conversations, investigative series, and stories that matter — anytime, anywhere.

Live Activity Update.

0

Competitions

0

Events

1

Polls

Featured Content

Your favourite in one place — stay updated and in the running.

More Presenters

The voices behind Channel Africa — passionate storytellers, journalists, and broadcasters from across the continent.

Boa noite! É quarta-feira e estamos prontos para mais uma edição do #Caleidoscópio com todas as últimas notícias.

#ChannelAfrica

Boa noite! É quarta-feira e estamos prontos para mais uma edição do #Caleidoscópio com todas as últimas notícias.

#ChannelAfrica

#ZOCHITIKA

MU NKHANI ZATHU ZA CHUMA

##Meyala wa mzinda wa Johannesburg mchigawo cha Gauteng mdziko la South Africa, Dada Morero, yati magalimoto oyendera mphamvu ya magetsi ali ndi kuthekera kothandiza nzika kuchepetsa kugwiritsira ndalama pa kugula mafuta a galimoto. Morereo, ...walankhula izi pa msonkhano otchedwa Electric Vehicle testing stations, pomwe wati nzika zikuyenera kuganiza za kuyamba kugwiritsira ntchito magalimoto oyendera magetsi.


#Bungwe loona zintchito za kufalitsa mau mdziko la Namibia, lakana kupereka chiphatso kukampani ya Starlink yomwe mwini wake ndi Elon Musk. Bungweli, lati lakana kupereka chiphatso ku kampaniyi yoyambira zintchito zake mdzikolo ati pa chifukwa cholephera kukwaniritsa kuperaka mapepala ena ofunika.

#Presidenti wa dziko la Kenya, William Ruto, wati boma lake lasaina mgwirizano ndi dziko la China pa nkhani za malonda. Mgwirizanowu, wasainidwa patadutsa miyezi iwiri potsatira kulengezedwa kwa mgwirizano wina ndi dziko la China ofikitsa malonda ku dzikolo mosapereka misonkho. Nkhani za malonda pakati pa maiko awiriwa zalimbikitsidwa potsatira Ruto kutenga ulendo ku dziko la China chaka chatha, komwe migwirizano ingapo inasainidwa.

#Unduna wa za chuma mdziko la Uganda, wati chuma cha dzikolo chinakwera ndi 8.5 percenti kumapeto kwa mwezi wa Disembala chaka chatha. Undunawu, wati uku kunali kukwera kusiyana ndi 5.4 percenti mu nyengo yomweyi mu chaka cha 2024. Undunawu, waonjezeranso kunena kuti kukweraku kunadza potsatira kukwera kwa zintchito mu gawo la zomangamanga. Kukhazikitsa kwa paipi ya mafuta yotalika ndi 143 kilomitsa, ya ndalama yokwana $5 billion, kwathandiza kukweza chuma cha dzikolo. Paipiyi, ikufikitsa mafuta kuchokera mdzikolo kukafika ku doko la Tanga mdziko la Tanzania.

Thamo Kapisa
Channel Africa News

#ZOCHITIKA

NKHANI ZATHU ZA LERO PA CHINYANJA SERVICE

#Dziko la Iran lati dziko la United States of America likungolankhula lokha, ndipo palibe nthumwi ya dziko la Iran yomwe ili pa zokambirana pa nkhani ya mikiangano yomwe ikuchitika pakati pa maikowa. Dzulo, Presidenti wa dziko ...la USA Donald Trump, analengeza kudzera pa tsamba lake la mchezo la Truth Social, kuti maikowa anali pa zokambirana ndipo agwirizana za kuimitsa kaye nkhondoyi. Mneneri mu unduna wa asilikali mdziko la Iran, Ebrahim Zoilfaghari, wati palibe zokambirana zina zilizonse zomwe zachitika, ndipo walankhula izi kudzera pa kanema wa pa intaneti.
Mtolankhani wa BBC Joanna Keane, wafotokoza kunena kuti mu kanemayu, mneneriyu saanatchule dzina koma walankhula mau ochenjeza mtsogoleri wa dziko la mphamvu kwambiri kuti dziko la Iran silingabvomelezane ndi mtsogoleri ngati otereyu.


#Asilikali otsutsana ndi asilikali a boma la dziko la Sudan, adzudzulidwa pa mchitidwe ofuna kulanda mwa upandu chipatala chachikulu mchigawo cha East Darfur pa tsiku loyamba la Eid al Fitr. Bungwe loona za umoyo pa dziko lonse la WHO, lati chiwerengero cha nthu omwe aphedwa pa chiwembuchi chakwera kufika pa 70, ndipo ambiri omwe aphedwa ndi amai ndi ana komanso ogwira ntchito za mzipatala. Mtolankhani wa BBC Richards Kagoe, wafotokoza kunena kuti nthumwi za mu bungwe lotchedwa ECL Humanitarian Research Lab, lomwe ndi la mdziko la USA, zati pali umboni otsonyeza kuti asilikaliwa anaponya ma bomba atatu pa nthawi zosiyana pa chipatala cha Eldane Teaching Hospital, chomwe ndi chachikulu kwambiri mchigawochi.

#Wamkulu wapampando wa bungwe loyanjanitsa maiko a mu Africa, la African Union, Mahmoud Ali Youssouf, wasankha presidenti wakale wa dziko la Tanzania Jakaya Kikwete, kukhala nthumwi yapadera ku chigawo cha Horn Of Africa komanso ku chigawo cha nyanja ya Red Sea. Kikwete, akuyembekezeka kulimbikitsa ntchito za bungweli maka pa nkhani za mikangano , bata ndi mtendere, koamanso chitetezo. Mtolankhani wa SABC Khayelihle Khumalo wafotokoza kunena kuti bungwe la AU lili ndi chikhulupiliro kuti Kikwete athandiza pa zintchitozi.

#Nthambi yowona ngozi zogwa mwadzidzidzi mdziko la Malawi ya DoDMA, yati mvula yamphamvu yomwe inagwa kuyambira pa 15 mpaka pa 19 March chaka chino m'madera osiyanasiyana, yakhudza mabanja osachepera 69,000.
Komishonala wa nthambiyi a Wilson Moleni ati mvulayi yakhudza makhonsolo 23, pamene anthu okwana makumi atatu amwalira, komanso kubalalisa mabanja okwana 3,900.
A Moleni ayankhula izi lero munzinda wa Lilongwe pa mkumano wachisanu okambilana nkhani yokhudza kuwonongeka kwa katundu m'mayiko a mu Africa kutsatira kuwonongeka kwa zachilengedwe.
Mlendo olemekezeka pa mwambowu ndi nduna yoona zachilengedwe ndikusintha kwa nyengo a Patricia Wiskes.
Mkumanowu omwe ukuyembekezeka kufika kumapeto pa 27 Marichi, ukuchitikira pa mutu oti "Kupititsa patsogolo ntchito yopeleka thandizo komanso upangiri ku mayiko aku Africa pofuna kuthana ndi kutaya katundu kaamba kakusintha kwa nyengo".

#Dziko la Ghana, lasaina mgwirizano ndi bungwe la European Union, pa nkhani za chitetezo, poona kuti zigawenga zikulimbikira mchitidwe wa ziwembu mmaiko a mchigawo cha kummadzulo kwa Africa.
Mgwirizanowu wasainidwa pa mwambo omwe wachitikira mu mzinda wa Accra mu likulu la dziko la Ghana. Wachiwiri kwa presidenti wa dziko la Ghana, Naana Opoku, pamodzi ndi mkulu wa nthambi yoona zintchito za chitetezo mu bungwe la EU, Ursula Kallas, ndi omwe anatsogolera mwambowu. Dziko la Ghana, lakhala dziko loyamba mu Africa kusaina mgwirizano otere ndi bungweli. Ngakhale dzikoli silinaukiridwe ndi zigawenga, maiko oyandikana ndi dzikolo akukhudzidwa kwambiri maka kuukiridwa ndi zigawenga za mgulu la Al Qaeda.

Thamo Kapisa
Channel Africa News

Join Mariamo Hassamo on #Caleidoscopio – a News and Current Affairs show that provides the latest updates on major news stories.

The show covers breaking stories as we round up all the news events of the day, especially on the African Continent between 20:00 – 21:00 CAT
...#ChannelAfrica

Imvani nkhani zabwino zapamwamba mwatsatane tsatane madzulo ano ndi Thamo Kapisa.

#Zochitika #ChannelAfrica #Chinyanja #ChinyanjaNewsBulletin

Muli bwanji Africa.
Ndi nthawi ya #Zochitika ndi Mada Phiri.

Fikani kuti mukhale mukudziwa zomwe zikuchitika mu Africa ndi padziko lonse lapansi.

#ChannelAfrica